Home National NTCHITO YOIKA CHLORINE MMIJIGO IKUPINDULA M’BOMA LA MANGOCHI.

NTCHITO YOIKA CHLORINE MMIJIGO IKUPINDULA M’BOMA LA MANGOCHI.

by Angaliba
6 views
Ngati njira imodzi yopititsa patsogolo ntchito yopereka madzi aukhondo m’boma la Mangochi bungwe lotchedwa Evedence Action likugwira ntchito yoika mankhwala a Chlorine mmijingo.
Poyendera ntchitoyi mdera la Namiyasi lowelukali wachiwiri wa nduna ya zaumoyo Halima Daudi wayamikira ntchitoyi kunena kuti ikuthandiza kulimbana ndi matenda otsekula mmimba omwe amavuta m’bomali.
Polankhula ndi Angaliba Daudi anati izi zikuthandiza kuti anthu azimwa madzi otetezeka zomwe zipititse patsogolo thanzi lao.
Mmodzi mwa anthu omwe akupindula ndi ntchitoyi Magret Ajidu anathokoza adindo powaganizira ndi ndondomekoyi yomwe anati ikupindulila anthu ochuluka omwe amagwiritsa ntchito mijigo.
Padakali pano Evidence Action ikugwira ntchitoyi mmaboma 8 mdziko muno ndipo bungweri lakwanitsa kale kuika makina otulutsa chlorine opitilila 16,000.
Wolemba; Blessings Kaimira. (Mangochi)

You may also like

ABOUT

ANGALIBA TV and FM is a cultural station with audiences across Malawi and beyond. Our programs champion meaningful communication for development through “mindset change” and by understanding culture through best education design systems in order to attain meaningful but sustainable socio-economic development.

Angaliba is a theme-based channel and radio station. 

Edtior's Picks

CONTACT US

Ginnery Corner, Opposite NBS Bank, Blantyre, Malawi
 
+265 999 95 82 06
+265 888 95 82 06
 
info@angaliba.africa
 
www.angaliba.africa
 
 

This website uses cookies to improve your experience. We'll assume you're ok with this, but you can opt-out if you wish. Accept Read More