“TISANGALALE MOYENERA” _ZAMBEZI EVANGELICAL CHURCH

Date:

Pomwe anthu a chipembedzo cha chi_khristu akusangalalila kubadwa kwa Yesu pa 25 December, mpingo wa Zambezi Evangelical Church (ZEC) wapempha a Malawi kuti apewe zoipa pa nyengoyi.
Polankhula ndi Angaliba wachiwiri wa mlembi wamkulu wa mpingowu Reverend Innocent Mlelele Wachimwa wati zambiri zimakhala zikuchitika mu mdzina la chisangalalo koma zina sizikhala zolingana ndi zimene zimafunikira pa tsiku la Khrismasi.
Iwo anati ena amatenga mwayi wa tsikuli kuchita zoipa monga ndeu,kuledzera, chiwerewere ndi kuba kungotchula zochepa chabe zomwe anati mzolakwika.
“Iyi ndi nthawi yowonetserana chikondi pakuti Yesu anabwera kudzakhala Chikondi pakati pathu” Anatelo a Reverend Wachimwa.
Chomcho iwo amema a Malawi kuti patsikuli awonetsetse kuti asangalale moyenera.
Malingana ndi Reverend Wachimwa, Patsikuli anthu ampingo wa Zambezi Evangelical amakhala a kupemphera mmipingo yawo yomwe ikupezeka mzigao zonse za dziko la Malawi komaso maiko akunja.

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

Share post:

Subscribe

spot_imgspot_img

Popular

More like this
Related

TNM Super League Match Sets Record with K113.7 Million Revenue, Spurs Calls for Improved Gate

The Super League of Malawi (Sulom) has expressed delight...

Mankhokwe Primary School Restores Sanitation with New Toilets After Cyclone Damage

Teachers and learners at Mankhokwe Primary School in Nsanje...

Farmers Trained in Sweet Potato Production and Value Addition

The University of Malawi (Unima), through its Centre for...
Verified by MonsterInsights